Zikomo Yesu – by The QFM

M'malo moti tizinyinyirika ndi mauthenga a kukonzanso (Reform Messages), bwanji tiyambe kumuthokoza Mulungu wathu kaamba ka mphatso yapaderadera ngati imeneyiyi, imene siinaperekedwe kwa wina aliyense pa dziko lino, koma kwa ife tokha basi!... Ndi zomvetsa chisoni kuti ambiri mmalo molandira ndi mtima wonse mauthenga okonzanso-wa, timanyalanyaza (monga ana a Israel) ndi kumuonetsa Mulungu ngati opanda nzeru potiuza zoyenera anthu Ake kuchita... komano tikanadziwa chikondi ndi ma plan a Mulungu wathu wachifundoyo — pa ife ana Ake, bwenzi tikungonena kuti "Zikomo Yesu" pa zinthu zonse zomwe Akutichitira, podziwa kuti Akuchita zonse ku ubwino wathu!