Mau Ofatsa – by The QFM

Pali kuyankhula kwamphamvu kwambiri kuposa kulankhula bwino kwa mawu mu moyo wabata, wokhazikika wa Mkristu woona, woyera. Zomwe munthu ali zimakhala ndi mphamvu zambiri kuposa zomwe akunena. MH 469.1 Alonda amene anatumidwa kwa Yesu anabwerako ndi mbiri yakuti palibe munthu analankhula monga Iye analankhula. Koma chifukwa cha ichi chinali chakuti palibe munthu anakhalapo monga Iye anakhala. Moyo Wake ukanakhala wina kuposa momwe unaliri, Iye sakanayankhula monga Iye anachitira. Mau ake anali ndi mphamvu yokhutiritsa, chifukwa anachokera mu mtima wangwiro ndi woyera, wodzala ndi chikondi ndi chisoni, kukoma mtima ndi choonadi. MH 469.2